আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা

পৃষ্ঠা নং:close

external-link copy
30 : 47

وَلَوۡ نَشَآءُ لَأَرَيۡنَٰكَهُمۡ فَلَعَرَفۡتَهُم بِسِيمَٰهُمۡۚ وَلَتَعۡرِفَنَّهُمۡ فِي لَحۡنِ ٱلۡقَوۡلِۚ وَٱللَّهُ يَعۡلَمُ أَعۡمَٰلَكُمۡ

Ndipo tikadafuna tikadakuonetsa iwo (amene akuchitira kaduka Chisilamu) ndipo ukadawadziwa ndi zizindikiro zawo. Koma ndithu uwadziwa m’kayankhulidwe (kawo) kokometsa ndipo Allah akudziwa zochita zanu zonse. info
التفاسير:

external-link copy
31 : 47

وَلَنَبۡلُوَنَّكُمۡ حَتَّىٰ نَعۡلَمَ ٱلۡمُجَٰهِدِينَ مِنكُمۡ وَٱلصَّٰبِرِينَ وَنَبۡلُوَاْ أَخۡبَارَكُمۡ

Ndipo ndithu tikuyesani mayeso mpaka tiwaonetsere poyera (adziwike) amene akumenya nkhondo mwa inu (chifukwa cha dini) ndi opirira (pamavuto); ndi kuzionetsera poyera nkhani zanu (zochita zanu). info
التفاسير:

external-link copy
32 : 47

إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَصَدُّواْ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ وَشَآقُّواْ ٱلرَّسُولَ مِنۢ بَعۡدِ مَا تَبَيَّنَ لَهُمُ ٱلۡهُدَىٰ لَن يَضُرُّواْ ٱللَّهَ شَيۡـٔٗا وَسَيُحۡبِطُ أَعۡمَٰلَهُمۡ

Ndithu amene akana (Mtumiki {s.a.w}) ndi kuwatsekereza anthu ku njira ya Allah, ndi kutsutsana ndi Mtumiki chiongoko chitadziwika kwa iwo, sangamsautse Allah ndi chilichonse, koma adzawaonongera ntchito zawo. info
التفاسير:

external-link copy
33 : 47

۞ يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَطِيعُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُواْ ٱلرَّسُولَ وَلَا تُبۡطِلُوٓاْ أَعۡمَٰلَكُمۡ

E inu amene mwakhulupirira! Mvereni Allah ndiponso mvereni mtumiki (Wake) ndipo musaononge ntchito zanu. info
التفاسير:

external-link copy
34 : 47

إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَصَدُّواْ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ ثُمَّ مَاتُواْ وَهُمۡ كُفَّارٞ فَلَن يَغۡفِرَ ٱللَّهُ لَهُمۡ

Ndithu amene sadakhulupirire ndi kwatsekereza anthu kunjira ya Allah, kenako nkufa uku ali osakhulupirira Allah sadzawakhululukira (zolakwa zawo). info
التفاسير:

external-link copy
35 : 47

فَلَا تَهِنُواْ وَتَدۡعُوٓاْ إِلَى ٱلسَّلۡمِ وَأَنتُمُ ٱلۡأَعۡلَوۡنَ وَٱللَّهُ مَعَكُمۡ وَلَن يَتِرَكُمۡ أَعۡمَٰلَكُمۡ

Musafooke ndi kufuna chimvano, (koma menyanani ndi adani anu); inu ndinu opambana. Ndipo Allah ali nanu (pokuthangatani ndi kukupulumutsani,) ndipo sakuchepetserani (mphoto ya) ntchito zanu. info
التفاسير:

external-link copy
36 : 47

إِنَّمَا ٱلۡحَيَوٰةُ ٱلدُّنۡيَا لَعِبٞ وَلَهۡوٞۚ وَإِن تُؤۡمِنُواْ وَتَتَّقُواْ يُؤۡتِكُمۡ أُجُورَكُمۡ وَلَا يَسۡـَٔلۡكُمۡ أَمۡوَٰلَكُمۡ

Ndithu moyo wapadziko lapansi ndi masewera ndi chibwana. Ndipo ngati mukhulupirira ndi kudzipatula kumachimo (Allah) akupatsani malipiro anu, ndipo sakukupemphani chuma chanu. info
التفاسير:

external-link copy
37 : 47

إِن يَسۡـَٔلۡكُمُوهَا فَيُحۡفِكُمۡ تَبۡخَلُواْ وَيُخۡرِجۡ أَضۡغَٰنَكُمۡ

Ngati akadachifuna (kuchokera) kwa inu chumacho ndi kukuchulukitsirani (chopereka),mukadachita umbombo (ndi chumacho), ndipo akadatulutsira (poyera) kaduka kanu. info
التفاسير:

external-link copy
38 : 47

هَٰٓأَنتُمۡ هَٰٓؤُلَآءِ تُدۡعَوۡنَ لِتُنفِقُواْ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ فَمِنكُم مَّن يَبۡخَلُۖ وَمَن يَبۡخَلۡ فَإِنَّمَا يَبۡخَلُ عَن نَّفۡسِهِۦۚ وَٱللَّهُ ٱلۡغَنِيُّ وَأَنتُمُ ٱلۡفُقَرَآءُۚ وَإِن تَتَوَلَّوۡاْ يَسۡتَبۡدِلۡ قَوۡمًا غَيۡرَكُمۡ ثُمَّ لَا يَكُونُوٓاْ أَمۡثَٰلَكُم

Ha! Ndinu amene mukuitanidwa kuti mupereke (chuma) mu njira ya Allah. Koma alipo ena a inu akuumira ndipo amene akuumira akuzimana yekha. Allah Ngwachikwanekwane ndipo inu ndinu amphawi. Ngati munyoza (Chisilamu) ndi kubwerera m’mbuyo posakhulupirira) Allah adzabweretsa m’malo mwanu anthu ena; iwo sadzakhala ngati inu. info
التفاسير: