আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা

Tâ-Hâ

external-link copy
1 : 20

طه

Tâ-Hâ [271] info

[271] Allah wapamwamba wayamba Sura iyi ndi malembo awa awiri potchalenja omwe akutsutsa zoti Qur’an idachokera kwa Allah, kuti atalemba yawo Qur’an yomwe malembo ake omwewa omwe iwo akuwadziwa bwino ndipo amawayankhula.
Koma alephera kutalitali kulemba buku ndi nzeru zawo monga ili. Ndipo kulephera kwawo kulemba buku longa ili, ndiumboni kuti bukuli lidachokera kwa Allah.

التفاسير:

external-link copy
2 : 20

مَآ أَنزَلۡنَا عَلَيۡكَ ٱلۡقُرۡءَانَ لِتَشۡقَىٰٓ

Sitidakuvumbulutsire iwe Qur’an kuti uvutike (nayo). info
التفاسير:

external-link copy
3 : 20

إِلَّا تَذۡكِرَةٗ لِّمَن يَخۡشَىٰ

Koma kuti ikhale ulaliki ndi chikumbutso kwa yemwe akuopa (ndikudzichepetsa kwa Allah). info
التفاسير:

external-link copy
4 : 20

تَنزِيلٗا مِّمَّنۡ خَلَقَ ٱلۡأَرۡضَ وَٱلسَّمَٰوَٰتِ ٱلۡعُلَى

Chovumbulitsidwa chochokera kwa Yemwe adalenga nthaka ndi thambo lotukuka kumwamba. info
التفاسير:

external-link copy
5 : 20

ٱلرَّحۡمَٰنُ عَلَى ٱلۡعَرۡشِ ٱسۡتَوَىٰ

(Iye ndi Allah), Wachifundo Chambiri; pa Arsh (Mpando wachifumu) adakhazikika, (kukhazikika koyenerana ndi ulemelero Wake kopanda kukufanizira ndi kukhazikika kwa chilichonse; pakuti Iye salingana ndi chilichonse pa chikhalidwe ndi mbiri Zake). info
التفاسير:

external-link copy
6 : 20

لَهُۥ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَا وَمَا تَحۡتَ ٱلثَّرَىٰ

Zonse za kumwamba ndi za pansi ndi za pakati pake ndi za pansi pa nthaka, nza Iye. info
التفاسير:

external-link copy
7 : 20

وَإِن تَجۡهَرۡ بِٱلۡقَوۡلِ فَإِنَّهُۥ يَعۡلَمُ ٱلسِّرَّ وَأَخۡفَى

Ndipo ngati ulankhula mokweza mawu, (iwe munthu), ndithu Iye akudziwa zobisika ndi zobisika kwambiri (zomwe mwazibisa mu mtima mwanu).[272] info

[272] M’ndime iyi Allah akuuza munthu kuti Iye akudziwa zonse zimene munthu amayankhula mokweza mawu ndi zimene munthu amayankhula ndi anzake mobisa, ngakhalenso zomwe mtima wake umamnong’oneza.

التفاسير:

external-link copy
8 : 20

ٱللَّهُ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَۖ لَهُ ٱلۡأَسۡمَآءُ ٱلۡحُسۡنَىٰ

Allah! Palibe wopembedzedwa mwachoonadi koma Iye. Iye ali ndi maina abwino (ndi mbiri zabwinonso). info
التفاسير:

external-link copy
9 : 20

وَهَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ مُوسَىٰٓ

Ndipo kodi yakufika nkhani ya Mûsa? (Yomwe njododometsa)?[273] info

[273] Ibun Abbas adati: “Izi zidali choncho Musa pamene adakwaniritsa chipangano cha nthawi imene adapangana ndi m’neneri Shuaibu chakuti amuwetere mbuzi kwa zaka 8 kapena 10, adachoka ulendo kubwerera kwawo ku Iguputo pamodzi ndi banja lake; ndipo adasokera njira. Udali usiku wamdima wozizira. Adayesa kupekesa moto kuti awothe koma adalephera. Ndipo ali choncho, adangoona moto chapatali kumbali yakumanja kwa njira. Pamene adauona adauganizira kuti ndi moto weniweni, pomwe udali moto woyera wakuunika kwa Allah. Udali kuyaka mu mtengo wamasamba obiriwira. Ndipo adangomva Mbuye wake akumuitana: “E iwe Musa! Ine ndine Mbuye wako. Ndikukuyankhula; vula nsapato zako.”

التفاسير:

external-link copy
10 : 20

إِذۡ رَءَا نَارٗا فَقَالَ لِأَهۡلِهِ ٱمۡكُثُوٓاْ إِنِّيٓ ءَانَسۡتُ نَارٗا لَّعَلِّيٓ ءَاتِيكُم مِّنۡهَا بِقَبَسٍ أَوۡ أَجِدُ عَلَى ٱلنَّارِ هُدٗى

Pamene adaona moto adauza banja lake: “Yembekezani (pano); ndithu ndaona moto; mwina ndingakakutengereni chikuni chamoto (kuti muothe), kapena ndikapeza ondiongolera njira pa motopo. info
التفاسير:

external-link copy
11 : 20

فَلَمَّآ أَتَىٰهَا نُودِيَ يَٰمُوسَىٰٓ

Koma pamene adaudzera motowo Anaitanidwa (kuti), “E, iwe Mûsa! info
التفاسير:

external-link copy
12 : 20

إِنِّيٓ أَنَا۠ رَبُّكَ فَٱخۡلَعۡ نَعۡلَيۡكَ إِنَّكَ بِٱلۡوَادِ ٱلۡمُقَدَّسِ طُوٗى

Ndithu ine ndine Mbuye wako! Vula nsapato zakozo; ndithu iwe uli pa chigwa chopatulika, chotchedwa Tuwa.” info
التفاسير: