Iye ndi Yemwe adakulengani ndi dongo, kenako adaika nthawi (yothera cholengedwa chilichonse), ndi nthawi ina yodziwika kwa Iye (yomwe njoukitsira zolengedwa ku imfa). Ndipo pa izi inu (osakhulupirira) mukukaikira.
Ndipo Iye ndi Allah (Wopembedzedwa) kumwamba ndi pansi. Akudziwa za mkati mwanu ndi zakunja kwanu, ndipo akudziwa zimene mukupeza (kuchokera mzochitachita zanu, zabwino kapena zoipa).