ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - خالد إبراهيم بتيالا

رقم الصفحة:close

external-link copy
102 : 2

وَٱتَّبَعُواْ مَا تَتۡلُواْ ٱلشَّيَٰطِينُ عَلَىٰ مُلۡكِ سُلَيۡمَٰنَۖ وَمَا كَفَرَ سُلَيۡمَٰنُ وَلَٰكِنَّ ٱلشَّيَٰطِينَ كَفَرُواْ يُعَلِّمُونَ ٱلنَّاسَ ٱلسِّحۡرَ وَمَآ أُنزِلَ عَلَى ٱلۡمَلَكَيۡنِ بِبَابِلَ هَٰرُوتَ وَمَٰرُوتَۚ وَمَا يُعَلِّمَانِ مِنۡ أَحَدٍ حَتَّىٰ يَقُولَآ إِنَّمَا نَحۡنُ فِتۡنَةٞ فَلَا تَكۡفُرۡۖ فَيَتَعَلَّمُونَ مِنۡهُمَا مَا يُفَرِّقُونَ بِهِۦ بَيۡنَ ٱلۡمَرۡءِ وَزَوۡجِهِۦۚ وَمَا هُم بِضَآرِّينَ بِهِۦ مِنۡ أَحَدٍ إِلَّا بِإِذۡنِ ٱللَّهِۚ وَيَتَعَلَّمُونَ مَا يَضُرُّهُمۡ وَلَا يَنفَعُهُمۡۚ وَلَقَدۡ عَلِمُواْ لَمَنِ ٱشۡتَرَىٰهُ مَا لَهُۥ فِي ٱلۡأٓخِرَةِ مِنۡ خَلَٰقٖۚ وَلَبِئۡسَ مَا شَرَوۡاْ بِهِۦٓ أَنفُسَهُمۡۚ لَوۡ كَانُواْ يَعۡلَمُونَ

Ndipo adatsatira njira za afiti zomwe asatana adali kuwafotokozera m’nthawi ya ufumu wa Sulaiman. Ndipo Sulaiman sadamkane Allah (sadali mfiti), koma asatana ndi amene adamkana, naphunzitsa anthu ufiti (umene adaudziwa kuyambira kale); natsatiranso (njira za ufiti) zimene zinatsitsidwa kwa Angelo awiri Haruta ndi Maruta (ku midzi ya) ku Babulo. Koma Angelowo sadaphunzitse aliyense pokhapokha atamuuza kuti: “Ife ndife mayeso (ofuna kuona kugonjera kwanu malamulo a Allah); choncho musamkane (Allah).” Komabe ankaphunzira kwa iwo njira zolekanitsira pakati pa munthu ndi mkazi wake, (ndi zina zotero). Ndipo sadavutitse aliyense ndi zimenezo koma mwachilolezo cha Allah. Ndipo akuphunzira zomwe zingawavutitse pomwe sizingawathandize. Ndithudi, akudziwa kuti yemwe wausankha (ufitiwo) sadzakhala ndi gawo lililonse (la zinthu zabwino) tsiku lachimaliziro. Ndithudi, nchoipitsitsa chimene adzisankhira okha akadakhala akudziwa. info
التفاسير:

external-link copy
103 : 2

وَلَوۡ أَنَّهُمۡ ءَامَنُواْ وَٱتَّقَوۡاْ لَمَثُوبَةٞ مِّنۡ عِندِ ٱللَّهِ خَيۡرٞۚ لَّوۡ كَانُواْ يَعۡلَمُونَ

Ndipo iwo akadakhulupirira nadzitchinjiriza (ku zoletsedwa), ndithudi, mphoto yochokera kwa Allah ikadakhala yabwino kwa iwo, akadadziwa. info
التفاسير:

external-link copy
104 : 2

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَقُولُواْ رَٰعِنَا وَقُولُواْ ٱنظُرۡنَا وَٱسۡمَعُواْۗ وَلِلۡكَٰفِرِينَ عَذَابٌ أَلِيمٞ

E inu amene mwakhulupirira! Musam’nenere (Mneneri liwu lakuti) “raina” (ndicholinga chomunenera kuti iye ndi mbutuma), koma mnenereni (liwu lakuti) “utiyang’anire,” ndipo mverani malamulo. Kwa osakhulupirira kuli chilango chopweteka. info
التفاسير:

external-link copy
105 : 2

مَّا يَوَدُّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ وَلَا ٱلۡمُشۡرِكِينَ أَن يُنَزَّلَ عَلَيۡكُم مِّنۡ خَيۡرٖ مِّن رَّبِّكُمۡۚ وَٱللَّهُ يَخۡتَصُّ بِرَحۡمَتِهِۦ مَن يَشَآءُۚ وَٱللَّهُ ذُو ٱلۡفَضۡلِ ٱلۡعَظِيمِ

Amene sadakhulupirire mwa anthu a mabuku (Ayuda ndi Akhirisitu) ndi omphatikiza Allah (Arabu), safuna kuti chabwino chilichonse chochokera kwa Mbuye wanu chitsitsidwe kwa inu (Asilamu). Koma Allah amamsankhira chifundo Chake amene wamfuna. Ndipo Allah ndi Mwini ubwino ochuluka. info
التفاسير: