పవిత్ర ఖురాన్ యొక్క భావార్థాల అనువాదం - చిచియో అనువాదం - ఖాలిద్ ఇబ్రాహీమ్ బైతాలా

Al-A’lâ

external-link copy
1 : 87

سَبِّحِ ٱسۡمَ رَبِّكَ ٱلۡأَعۡلَى

Lemekeza dzina la Mbuye wako Wapamwambamwamba (ndikuliyeretsa ku zinthu zosayenera).[417] info

[417] Tanthauzo lakulemekeza dzina la Allah ndiko kukhulupilira kuti iye ndiwopatulika ku mbiri zilizonse zoipa zosamuyenera, monga kumufanizira ndizolengedwa; monga kuti anabereka kapena adaberekedwa, kapena kuti ali ndi mkazi kapenanso kuti alipo omwe amathandizana naye pa Umulungu Wake.

التفاسير:

external-link copy
2 : 87

ٱلَّذِي خَلَقَ فَسَوَّىٰ

Amene adalenga (chilichonse) ndikuchikonza bwinobwino (mkalengedwe kolingana). info
التفاسير:

external-link copy
3 : 87

وَٱلَّذِي قَدَّرَ فَهَدَىٰ

Amene adalamuliratu (chilichonse zochita zake) ndi kuchiongolera.[418] info

[418] Allah pambuyo polenga zolengedwa Zake sadangozileka kuti zisadziwe chochita, koma cholengedwa chilichonse adachilamuliratu kuti chichite zoyenera nacho, ndipo pambuyo pake adachiongolera pa chinthu chimenecho; chidadziwa, ndipo chidachita. Munthu adamusonyeza zomwe zili ndi mazunzo mkati mwake kuti adzitalikitse nazo ndiponso adamusonyeza zabwino kuti azichite.

التفاسير:

external-link copy
4 : 87

وَٱلَّذِيٓ أَخۡرَجَ ٱلۡمَرۡعَىٰ

Ndi Yemwenso akumeretsa msipu. info
التفاسير:

external-link copy
5 : 87

فَجَعَلَهُۥ غُثَآءً أَحۡوَىٰ

Ndipo nausandutsa kukhala wouma ndi wodera. info
التفاسير:

external-link copy
6 : 87

سَنُقۡرِئُكَ فَلَا تَنسَىٰٓ

Tikulakatulira (chivumbulutso Chathu) ndipo siuyiwala.[419] info

[419] Mneneri Muhammad (s.a.w) adali munthu monga anthu ena ndipo adali ndi mbiri zonga anthu adalinazo, monga: kukonda ndi kusakonda, kuiwala ndi kukumbukira. Padapezeka kuti nthawi ina adaiwala ndi kupemphera maraka atatu m’Swala ya maraka anayi. Pachifukwa ichi pa nthawi yovumbulutsidwa Qur’an ndi Jibril, adali akubwereza bwereza mawu ovumbulutsidwawo kuopa kuti angaiwale. Choncho, apa Allah akumuletsa kuti asadzivutitse kumabwerezabwereza mawuwo pamene akuvumbulutsidwa ndipo adamupatsa lonjezo nthawi yomweyo kuti sadzaiwala. Ndipo adakwaniritsa lonjezo Lake. Mtumiki (s.a.w) adali kumtsikira ma surah aataliatali ndipo amatha kuwawerenga (molakatula) popanda kuonjezera kanthu kapena kuchepetsa, ngakhale kuti iye sadali kudziwa kuwerenga ndi kulemba. Kuwerenga kwake kudali kwakungolakatula pa mtima.

التفاسير:

external-link copy
7 : 87

إِلَّا مَا شَآءَ ٱللَّهُۚ إِنَّهُۥ يَعۡلَمُ ٱلۡجَهۡرَ وَمَا يَخۡفَىٰ

Kupatula chimene wafuna Allah (kuti uchiiwale); ndithu Iye amadziwa zoonekera ndi zimene zimabisika. info
التفاسير:

external-link copy
8 : 87

وَنُيَسِّرُكَ لِلۡيُسۡرَىٰ

Ndipo tikufewetsera (njira yochitira zinthu) zabwino.[420] info

[420] Tanthauzo la ‘kufewetsa’ ndiko kuti Shariya ya Chisilamu (malamulo) siili yovuta kuyikwaniritsa monga momwe adalili malamulo a zipembedzo zoyamba. Ndipo ndi malamulo othandiza anthu onse, nthawi zonse ndi pamalo paliponse.

التفاسير:

external-link copy
9 : 87

فَذَكِّرۡ إِن نَّفَعَتِ ٱلذِّكۡرَىٰ

Choncho akumbutse (wanthu powalalikira) ngati kukumbutsa kuthandiza.[421] info

[421] Tanthauzo la apa sikuti Mtumiki (s.a.w) alalikire pokhapokha waona kuti ulalikiwo uthandiza ayi, koma alalikire ndithu kaya kulalikirako kuthandiza kapena ayi, monga momwe zalongosolera Ayah zotsatirazi. Kuyankhula kotere, Arabu amakutcha “iktifa.”

التفاسير:

external-link copy
10 : 87

سَيَذَّكَّرُ مَن يَخۡشَىٰ

(Palibe chikaiko ulalikiwo) aukumbukira (ndikuthandizidwa nawo) amene akuopa Allah. info
التفاسير: