அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா

At-Taubah

external-link copy
1 : 9

بَرَآءَةٞ مِّنَ ٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦٓ إِلَى ٱلَّذِينَ عَٰهَدتُّم مِّنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ

Uku ndikudzipatula kochokera kwa Allah ndi Mtumiki wake ku (mapangano) amene mudapangana nawo (kenako nkuswa mapangano awowo) a m’gulu la Amushirikina.[204] info

[204] (Ndime 1-2) Omasulila Qur’an adati Arabu adali kuswa mapangano amene adamanga pamodzi ndi Mtumiki wa Allah. Potero, Allah adalamula Mtumiki Wake kuti awaponyere mapangano awo. Choncho, Mtumiki adatuma Abubakari (r.a) kukhala mtsogoleri wa anthu kumapemphero a Hajj. Ndipo adamtsatanso Ali (r.a) kumeneko ndi nkhani yokhayokhayo kuti akawawerengere anthu kuti Allah ndi Mtumiki Wake atulukamo m’mapangano okhalirana mwa mtendere ndi Amushirikina sadzaloledwa kuyandikira Nyumba Yopatulika chaka chotsatiracho, ndikutinso sadzaloledwa kuzungulira Nyumba yopatulikayo uku ali maliseche.

التفاسير:

external-link copy
2 : 9

فَسِيحُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ أَرۡبَعَةَ أَشۡهُرٖ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّكُمۡ غَيۡرُ مُعۡجِزِي ٱللَّهِ وَأَنَّ ٱللَّهَ مُخۡزِي ٱلۡكَٰفِرِينَ

(Auze Amushirikina kuti): Yendani pa dziko miyezi inayi basi. (Pambuyo pake sipadzakhala chitetezo pakati pawo ndi ife). Ndipo dziwani kuti inu simungathe kumpambana Allah. Ndipo Allah Ngosambula osakhulupirira. info
التفاسير:

external-link copy
3 : 9

وَأَذَٰنٞ مِّنَ ٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦٓ إِلَى ٱلنَّاسِ يَوۡمَ ٱلۡحَجِّ ٱلۡأَكۡبَرِ أَنَّ ٱللَّهَ بَرِيٓءٞ مِّنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ وَرَسُولُهُۥۚ فَإِن تُبۡتُمۡ فَهُوَ خَيۡرٞ لَّكُمۡۖ وَإِن تَوَلَّيۡتُمۡ فَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّكُمۡ غَيۡرُ مُعۡجِزِي ٱللَّهِۗ وَبَشِّرِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ بِعَذَابٍ أَلِيمٍ

Ndipo uku ndi kulengeza kochokera kwa Allah ndi Mtumiki Wake kwa Anthu pa tsiku la Hajj yaikulu kuti ndithu Allah ndi Mtumiki Wake adzichotsa mmapangano a Amushirikina (omwe ali achinyengo). Choncho, ngati mulapa ndibwino kwa inu; ndipo ngati mutembenuka ndi kunyoza, dziwani kuti inu simungamulepheretse Allah. Ndipo auze za chilango chowawa amene sadakhulupirire. info
التفاسير:

external-link copy
4 : 9

إِلَّا ٱلَّذِينَ عَٰهَدتُّم مِّنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ ثُمَّ لَمۡ يَنقُصُوكُمۡ شَيۡـٔٗا وَلَمۡ يُظَٰهِرُواْ عَلَيۡكُمۡ أَحَدٗا فَأَتِمُّوٓاْ إِلَيۡهِمۡ عَهۡدَهُمۡ إِلَىٰ مُدَّتِهِمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ يُحِبُّ ٱلۡمُتَّقِينَ

Kupatula ena amene mudapangana nawo mapangano mwa Amushirikina, (omwe adasunga mapangano awo), kenako sadapungule chilichonse ndipo sadathandize aliyense pa inu, akwaniritseni mapangano awo mpaka m’nyengo yawo. Ndithu Allah akukonda amene akumuopa (ndi kusunga mapangano). info
التفاسير:

external-link copy
5 : 9

فَإِذَا ٱنسَلَخَ ٱلۡأَشۡهُرُ ٱلۡحُرُمُ فَٱقۡتُلُواْ ٱلۡمُشۡرِكِينَ حَيۡثُ وَجَدتُّمُوهُمۡ وَخُذُوهُمۡ وَٱحۡصُرُوهُمۡ وَٱقۡعُدُواْ لَهُمۡ كُلَّ مَرۡصَدٖۚ فَإِن تَابُواْ وَأَقَامُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتَوُاْ ٱلزَّكَوٰةَ فَخَلُّواْ سَبِيلَهُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٞ

Ndipo miyezi yopatulika ikatha (yomwe njoletsedwa kuchitamo nkhondo), apheni Amushirikina paliponse pamene mwawapeza (menyanani nawo), ndipo agwireni (monga momwe iwo akukuchitirani). Ndipo azungulireni ndi kuwakhalira pa njira zonse. Koma akalapa nayamba kupemphera Swala, ndikupereka chopereka (Zakaat), ilekeni njira yawoyo (asiyeni). Ndithu Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha. info
التفاسير:

external-link copy
6 : 9

وَإِنۡ أَحَدٞ مِّنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ ٱسۡتَجَارَكَ فَأَجِرۡهُ حَتَّىٰ يَسۡمَعَ كَلَٰمَ ٱللَّهِ ثُمَّ أَبۡلِغۡهُ مَأۡمَنَهُۥۚ ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ قَوۡمٞ لَّا يَعۡلَمُونَ

Ndipo ngati mmodzi wa Amushirikina Atakupempha chitetezo (kuti amvere mawu a Allah), mtetezeni kuti amve mawu a Allah. Kenako (ngati sadakhutitsidwe nawo), mpititseni kumalo kwake mwamtendere (ngati safuna kulowa m’Chisilamu). Izi nchifukwa chakuti iwo ndi anthu osadziwa. info
التفاسير: