அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா

பக்க எண்:close

external-link copy
6 : 11

۞ وَمَا مِن دَآبَّةٖ فِي ٱلۡأَرۡضِ إِلَّا عَلَى ٱللَّهِ رِزۡقُهَا وَيَعۡلَمُ مُسۡتَقَرَّهَا وَمُسۡتَوۡدَعَهَاۚ كُلّٞ فِي كِتَٰبٖ مُّبِينٖ

۞ Ndipo palibe nyama iliyonse panthaka koma rizq lake lili kwa Allah; ndipo (Iye) akudziwa mbuto yake yamuyaya ndi mbuto yake yakungodutsapo (yomwe ndi pano padziko lapansi). Zonse zili m’buku lofotokoza chilichonse.[219] info

[219] Mawu oti “Riziki lake lili kwa Allah’’ nkuti Allah wapatsa chilichonse mphamvu zofunira riziki lake (zoyendetsa moyo wake). Ndimeyi siitanthauza kuti munthu angokhala popanda kugwira ntchito nayembekezera kuti riziki lichokera kumwamba. Koma munthu agwire ntchito molimbikira kuti apeze chuma cha Allah. Zotere nzimene Qur’an ikutilangiza.

التفاسير:

external-link copy
7 : 11

وَهُوَ ٱلَّذِي خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ فِي سِتَّةِ أَيَّامٖ وَكَانَ عَرۡشُهُۥ عَلَى ٱلۡمَآءِ لِيَبۡلُوَكُمۡ أَيُّكُمۡ أَحۡسَنُ عَمَلٗاۗ وَلَئِن قُلۡتَ إِنَّكُم مَّبۡعُوثُونَ مِنۢ بَعۡدِ ٱلۡمَوۡتِ لَيَقُولَنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُوٓاْ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا سِحۡرٞ مُّبِينٞ

Ndipo Iye ndi Yemwe adalenga thambo ndi nthaka m’masiku asanu ndi limodzi, ndipo Arsh Yake (Mpando Wake wachifumu) idali pa madzi. (Adakulengani) kuti akuyeseni mayeso, ndani mwa inu ali wochita zabwino. Koma ukanena (kwa iwo kuti): “Inu mudzaukitsidwa pambuyo pa imfa,” amene sadakhulupirire akuti: “Izi sikanthu koma ndi matsenga oonekera.”[220] info

[220] Kunena kwakuti thambo ndi nthaka zidalengedwa m’masiku asanu ndi limodzi, amene akudziwa za masiku asanu ndi limodziwo momwe adalili ndi Allah yekha. Ndiponso mpandowo sitikudziwa tsatanetsatane wake. Chimene chilipo kwa ife nkukhulupilira basi.

التفاسير:

external-link copy
8 : 11

وَلَئِنۡ أَخَّرۡنَا عَنۡهُمُ ٱلۡعَذَابَ إِلَىٰٓ أُمَّةٖ مَّعۡدُودَةٖ لَّيَقُولُنَّ مَا يَحۡبِسُهُۥٓۗ أَلَا يَوۡمَ يَأۡتِيهِمۡ لَيۡسَ مَصۡرُوفًا عَنۡهُمۡ وَحَاقَ بِهِم مَّا كَانُواْ بِهِۦ يَسۡتَهۡزِءُونَ

Ndipo ngati titawachedwetsera chilango mpaka m’nthawi yodziwika (ndi kukhazikitsidwa ndi Ife), akunena (mwamwano): “Nchiyani chikumanga chilangocho (kuti chidze)? “Tamverani! Tsiku lomwe chidzawadzera, sichidzachotsedwa kwa iwo ndipo zomwe adali kuzichita mwachibwana zidzawazinga. info
التفاسير:

external-link copy
9 : 11

وَلَئِنۡ أَذَقۡنَا ٱلۡإِنسَٰنَ مِنَّا رَحۡمَةٗ ثُمَّ نَزَعۡنَٰهَا مِنۡهُ إِنَّهُۥ لَيَـُٔوسٞ كَفُورٞ

Ndipo munthu tikamulawitsa mtendere wochokera kwa Ife, kenako nkuuchotsa kwa iye, ndithu amakhala wotaya mtima kwambiri ndikukhala wosathokoza. info
التفاسير:

external-link copy
10 : 11

وَلَئِنۡ أَذَقۡنَٰهُ نَعۡمَآءَ بَعۡدَ ضَرَّآءَ مَسَّتۡهُ لَيَقُولَنَّ ذَهَبَ ٱلسَّيِّـَٔاتُ عَنِّيٓۚ إِنَّهُۥ لَفَرِحٞ فَخُورٌ

Koma ngati titamulawitsa mtendere pambuyo pa masautso omwe adamkhudza, amati: “Masautso andichoka,”(ndipo sakhala wotanganidwa ndi ntchito zabwino zosonyeza kuyamika Allah), ndithudi iye amakhala wosangalala, wodzitukumula. info
التفاسير:

external-link copy
11 : 11

إِلَّا ٱلَّذِينَ صَبَرُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ أُوْلَٰٓئِكَ لَهُم مَّغۡفِرَةٞ وَأَجۡرٞ كَبِيرٞ

Koma amene apirira ndi kumachita ntchito zabwino, iwowo ndiwo adzapeza chikhululuko ndi malipiro aakulu (kwa Allah). info
التفاسير:

external-link copy
12 : 11

فَلَعَلَّكَ تَارِكُۢ بَعۡضَ مَا يُوحَىٰٓ إِلَيۡكَ وَضَآئِقُۢ بِهِۦ صَدۡرُكَ أَن يَقُولُواْ لَوۡلَآ أُنزِلَ عَلَيۡهِ كَنزٌ أَوۡ جَآءَ مَعَهُۥ مَلَكٌۚ إِنَّمَآ أَنتَ نَذِيرٞۚ وَٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ وَكِيلٌ

Mwina usiya zina mwa zomwe zikuvumbulutsidwa kwa iwe ndikubanika nazo mchifuwa mwako chifukwa chakuti akunena: “Bwanji sizidatsitsidwe kwa iye nkhokwe za chuma kapena bwanji mngelo osadza pamodzi ndi iye?” Koma ndithu iwe ndiwe mchenjezi basi ndipo Allah ndiye muyang’aniri wa chinthu chilichonse.[221] info

[221] Ophatikiza Allah ndi zina zake adali kupereka maganizo kwa Mtumiki akuti ampemphe Allah kuti adzetse milumilu ya chuma kapena amutumizire angelo kuti aziyenda naye limodzi. Ndipo adalinso kumaichitira Qur’an chibwana Mtumiki akawawerengera. Potero Mtumiki (s.a.w) adali kubanika mu mtima mwake akafuna kufikitsa uthenga kwa iwo chifukwa chakuopa kutsutsidwa ndi kumchitira chibwana.

التفاسير: