د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - خالد ابراهیم بتیالا

د مخ نمبر:close

external-link copy
28 : 23

فَإِذَا ٱسۡتَوَيۡتَ أَنتَ وَمَن مَّعَكَ عَلَى ٱلۡفُلۡكِ فَقُلِ ٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ ٱلَّذِي نَجَّىٰنَا مِنَ ٱلۡقَوۡمِ ٱلظَّٰلِمِينَ

Ndipo ukakhazikika m’chombocho, iwe ndi amene uli nawo, nena: “Tikuthokoza Allah, amene watipulumutsa ku anthu osalungama.” info
التفاسير:

external-link copy
29 : 23

وَقُل رَّبِّ أَنزِلۡنِي مُنزَلٗا مُّبَارَكٗا وَأَنتَ خَيۡرُ ٱلۡمُنزِلِينَ

Ndipo (potsika), nena: “E Mbuye wanga! Nditsitseni; kutsitsa kwa madalitso, pakuti Inu ndinu wotsitsa bwino kwambiri kuposa otsitsa.” info
التفاسير:

external-link copy
30 : 23

إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَٰتٖ وَإِن كُنَّا لَمُبۡتَلِينَ

Ndithu m’zimenezi muli zisonyezo. Ndithu Ife tili (ndi udindo) wowayesa ndi mayeso osiyanasiyana. info
التفاسير:

external-link copy
31 : 23

ثُمَّ أَنشَأۡنَا مِنۢ بَعۡدِهِمۡ قَرۡنًا ءَاخَرِينَ

Kenako tidabweretsa m’badwo wina pambuyo pawo (omwe ndi Âdi). info
التفاسير:

external-link copy
32 : 23

فَأَرۡسَلۡنَا فِيهِمۡ رَسُولٗا مِّنۡهُمۡ أَنِ ٱعۡبُدُواْ ٱللَّهَ مَا لَكُم مِّنۡ إِلَٰهٍ غَيۡرُهُۥٓۚ أَفَلَا تَتَّقُونَ

Ndipo tidatuma kwa iwo mtumiki (Hûd) wochokera mwa iwo, (yemwe ankati): “Pembedzani Allah! Mulibe mulungu wina kupatula Iye. Kodi simuopa? info
التفاسير:

external-link copy
33 : 23

وَقَالَ ٱلۡمَلَأُ مِن قَوۡمِهِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَكَذَّبُواْ بِلِقَآءِ ٱلۡأٓخِرَةِ وَأَتۡرَفۡنَٰهُمۡ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا مَا هَٰذَآ إِلَّا بَشَرٞ مِّثۡلُكُمۡ يَأۡكُلُ مِمَّا تَأۡكُلُونَ مِنۡهُ وَيَشۡرَبُ مِمَّا تَشۡرَبُونَ

Ndipo akuluakulu a mwa anthu ake amene adali osakhulupirira, ndikutsutsa za kukumana ndi tsiku la chimaliziro, omwe tidawapatsa kulemera pa moyo wa padziko lapansi, adati: “Uyu saali kanthu, koma ndi munthu monga inu; amadya zimene inu mumadya, ndi kumwa zomwe inu mumamwa. info
التفاسير:

external-link copy
34 : 23

وَلَئِنۡ أَطَعۡتُم بَشَرٗا مِّثۡلَكُمۡ إِنَّكُمۡ إِذٗا لَّخَٰسِرُونَ

Koma ngati mumvera munthu wonga inu, ndiye kuti mukhala otaika (oluza). info
التفاسير:

external-link copy
35 : 23

أَيَعِدُكُمۡ أَنَّكُمۡ إِذَا مِتُّمۡ وَكُنتُمۡ تُرَابٗا وَعِظَٰمًا أَنَّكُم مُّخۡرَجُونَ

Kodi akukulonjezani kuti mukadzafa ndikusanduka dothi ndi mafupa, mudzaukitsidwanso (m’manda)? info
التفاسير:

external-link copy
36 : 23

۞ هَيۡهَاتَ هَيۡهَاتَ لِمَا تُوعَدُونَ

Sizingachitike, sizingachitike, zimene mukulonjezedwazi! info
التفاسير:

external-link copy
37 : 23

إِنۡ هِيَ إِلَّا حَيَاتُنَا ٱلدُّنۡيَا نَمُوتُ وَنَحۡيَا وَمَا نَحۡنُ بِمَبۡعُوثِينَ

Palibe (moyo wina) koma moyo wathu wapadziko lapansiwu basi! Tikufa ndiponso kukhala ndi moyo! Ndipo sitidzaukitsidwa m’manda. info
التفاسير:

external-link copy
38 : 23

إِنۡ هُوَ إِلَّا رَجُلٌ ٱفۡتَرَىٰ عَلَى ٱللَّهِ كَذِبٗا وَمَا نَحۡنُ لَهُۥ بِمُؤۡمِنِينَ

Uyu saali kanthu (amene akudzitcha kuti ndi Mtumiki) koma ndi munthu basi, akupekera Allah bodza, ndipo ife sitimkhulupirira.” info
التفاسير:

external-link copy
39 : 23

قَالَ رَبِّ ٱنصُرۡنِي بِمَا كَذَّبُونِ

(Mtumikiyo) adati: “E Mbuye wanga! Ndipulumutseni pachifukwa chakuti anditsutsa.” info
التفاسير:

external-link copy
40 : 23

قَالَ عَمَّا قَلِيلٖ لَّيُصۡبِحُنَّ نَٰدِمِينَ

(Allah) adati: “Posachedwapa akhala odzinena.” info
التفاسير:

external-link copy
41 : 23

فَأَخَذَتۡهُمُ ٱلصَّيۡحَةُ بِٱلۡحَقِّ فَجَعَلۡنَٰهُمۡ غُثَآءٗۚ فَبُعۡدٗا لِّلۡقَوۡمِ ٱلظَّٰلِمِينَ

Choncho, mkuwe wa (chilango) choonadi udawaononga, ndipo tidawachita ngati zinyalala (zongotengedwa ndi madzi). Choncho, kuonongeka kudatsimikizika pa anthu osalungama. info
التفاسير:

external-link copy
42 : 23

ثُمَّ أَنشَأۡنَا مِنۢ بَعۡدِهِمۡ قُرُونًا ءَاخَرِينَ

Ndipo titatero tidalenga mibadwo ina pambuyo pawo. info
التفاسير: