[258] Ayuda adamufunsa Mneneri (s.a.w) zankhani ya anyamata a kuphangawo. Iye adayankha kuti: “Ndikuuzani mawa,” sadanene kuti Allah akafuna ndikuuzani mawa.”
Choncho chivumbulutso sichidadze kwa iye ndipo anavutika kwambiri kusowa chowauza anthu aja. Kenako Allah adamuuza zoti ngati unena pa chinthu kuti chimenechi ndichichita mawa, nenanso mawu oti ngati Allah afuna.