[43] Ibun Abbas adati anthuwo adali zikwi zinayi. Adatuluka m’nyumba zawo kuthawa mliri wanthomba, nati pakati pawo: “Tipite kudziko lina komwe kulibe mliri wanthomba.” Choncho adayenda mpaka kufika pamalo pena; ndipo Allah adati kwa iwo: “Mwalirani,” ndipo onse anamwaliradi nthawi yomweyo. Ndipo mmodzi wa aneneri adawadutsa iwo ali akufa, nampempha Allah kuti awawukitse kuti azimgwadira. Choncho adawaukitsa. Nkhaniyi tikuphunziramo zoti imfa siithawika.