पवित्र कुरअानको अर्थको अनुवाद - चेवा अनुवाद : खालिद इब्राहीम बेतियाला ।

external-link copy
35 : 8

وَمَا كَانَ صَلَاتُهُمۡ عِندَ ٱلۡبَيۡتِ إِلَّا مُكَآءٗ وَتَصۡدِيَةٗۚ فَذُوقُواْ ٱلۡعَذَابَ بِمَا كُنتُمۡ تَكۡفُرُونَ

Ndipo mapemphero awo pa nyumba yopatulikayo sadali kanthu, koma kuyimba miluzi ndi kuomba m’manja. Choncho (adzauzidwa): “Lawani chilango chifukwa chakusakhulupirira kwanu.” info
التفاسير: