[32] Ndime iyi ikuletsa Asilamu kukwatirana ndi anthu osakhulupilira Allah kupatula Akhirisitu ndi Ayuda. Nkosaloledwa mwamuna wa Chisilamu kukwatira mkazi wopembedza mafano. Nkosaloledwa kuti mkazi wa Chisilamu akwatiwe ndi mwamuna wopembedza mafano. Koma mwamuna wa Chisilamu atha kukwatira mkazi wa Chikhrisitu kapena wa Chiyuda pomwe mkazi wa Chisilamu saloledwa kukwatiwa ndi mwamuna wa Chikhrisitu kapena wa Chiyuda.