[211] M’ndime iyi Allah akutifotokozera magulu a anthu amene ngoyenera kuwagawira chuma cha Zakaat. Iwo ndi awa:- 1. Osauka amene sangagwire ntchito nkudzipezera okha chakudya (mafukara). 2. Osauka amene alibe zokwanira pa zofunikira pa moyo wawo (Masikini). 3. Amene akusonkhetsa chuma cha Zakaat cho omwe ntchito yawo ndiyokhayo. 4. Amene angolowa kumene m’Chisilamu omwe akuyembekezedwa kuti akapatsidwa adzalimbikitsidwa mitima yawo pa chipembedzochi. 5. Amene afuna kudziombola ku ukapolo. 6. Amene akulephera kulipira ngongole ya choonadi. 7. Amene akuchita Jihâd panjira ya Allah. 8. Wapaulendo amene alibe choyendera (ndalama zoyendera).