[352] M’ndime imeneyi Allah akunenetsa kuti: ‘‘Amene akukhulupilira mwa Allah ndi tsiku lachimaliziro, asapalane ubwenzi ndi munthu wodana ndi Allah ndi Mthenga Wake ngakhale wodana ndi Allah yo atakhala bambo wake, mwana wake ndi wina aliyense; apatukane nawo ndithu; chifukwa kupanda kutero akusonyeza kufooka kwa chikhulupiliro. Mtumiki (s.a.w) adati: “Munthu adzakhala ndi amene amamkonda pa tsiku la chiweruziro.”