क़ुरआन के अर्थों का अनुवाद - चेवा अनुवाद - ख़ालिद अबराहीम बेताला

पृष्ठ संख्या:close

external-link copy
87 : 12

يَٰبَنِيَّ ٱذۡهَبُواْ فَتَحَسَّسُواْ مِن يُوسُفَ وَأَخِيهِ وَلَا تَاْيۡـَٔسُواْ مِن رَّوۡحِ ٱللَّهِۖ إِنَّهُۥ لَا يَاْيۡـَٔسُ مِن رَّوۡحِ ٱللَّهِ إِلَّا ٱلۡقَوۡمُ ٱلۡكَٰفِرُونَ

“E ana anga! Pitani mukafufuzefufuze za Yûsuf ndi m’bale wake, ndipo musataye mtima pa chifundo cha Allah. Ndithu palibe amene amataya mtima za chifundo cha Allah koma anthu osakhulupirira.” info
التفاسير:

external-link copy
88 : 12

فَلَمَّا دَخَلُواْ عَلَيۡهِ قَالُواْ يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡعَزِيزُ مَسَّنَا وَأَهۡلَنَا ٱلضُّرُّ وَجِئۡنَا بِبِضَٰعَةٖ مُّزۡجَىٰةٖ فَأَوۡفِ لَنَا ٱلۡكَيۡلَ وَتَصَدَّقۡ عَلَيۡنَآۖ إِنَّ ٱللَّهَ يَجۡزِي ٱلۡمُتَصَدِّقِينَ

(Ndipo adapita ku Iguputo). Choncho pamene adalowa kwa iye (Yûsuf), adati: “E inu olemekezeka! Masautso atikhudza, ife ndi maanja athu; choncho tabwera ndi chuma chopanda pake. Tidzadzireni mlingo (ngakhale chuma chathucho chili chopanda pake), ndipo tithandizeni mwaulere. Ndithu Allah amawalipira othandiza mwaulere.” info
التفاسير:

external-link copy
89 : 12

قَالَ هَلۡ عَلِمۡتُم مَّا فَعَلۡتُم بِيُوسُفَ وَأَخِيهِ إِذۡ أَنتُمۡ جَٰهِلُونَ

(Iye) adati: “Kodi mukudziwa zomwe mudamchitira Yûsuf ndi m’bale wake pamene inu mudali mu umbuli?” info
التفاسير:

external-link copy
90 : 12

قَالُوٓاْ أَءِنَّكَ لَأَنتَ يُوسُفُۖ قَالَ أَنَا۠ يُوسُفُ وَهَٰذَآ أَخِيۖ قَدۡ مَنَّ ٱللَّهُ عَلَيۡنَآۖ إِنَّهُۥ مَن يَتَّقِ وَيَصۡبِرۡ فَإِنَّ ٱللَّهَ لَا يُضِيعُ أَجۡرَ ٱلۡمُحۡسِنِينَ

(Iwo) adati: “Kodi iwe ndiwe Yûsuf?” Adati: “Ine ndine Yûsuf, ndipo uyu ndi m’bale wanga; Allah watichitira zabwino. Ndithu amene aopa Allah ndikumapirira, (Allah amulipira). Ndithu Allah sasokoneza malipiro a ochita zabwino.” info
التفاسير:

external-link copy
91 : 12

قَالُواْ تَٱللَّهِ لَقَدۡ ءَاثَرَكَ ٱللَّهُ عَلَيۡنَا وَإِن كُنَّا لَخَٰطِـِٔينَ

(Iwo) adati: “Tikulumbira Allah! Allah wakusankha pa ife, ndipo ife tidalidi olakwa.” info
التفاسير:

external-link copy
92 : 12

قَالَ لَا تَثۡرِيبَ عَلَيۡكُمُ ٱلۡيَوۡمَۖ يَغۡفِرُ ٱللَّهُ لَكُمۡۖ وَهُوَ أَرۡحَمُ ٱلرَّٰحِمِينَ

(Iye) adati: “Lero palibe kukudzudzulani; Allah akukhulukirani, ndipo Iye Ngwachifundo chochuluka kuposa achifundo.” info
التفاسير:

external-link copy
93 : 12

ٱذۡهَبُواْ بِقَمِيصِي هَٰذَا فَأَلۡقُوهُ عَلَىٰ وَجۡهِ أَبِي يَأۡتِ بَصِيرٗا وَأۡتُونِي بِأَهۡلِكُمۡ أَجۡمَعِينَ

“Pitani ndi mkanjo wangawu ndipo mukauponye pamaso pa bambo wanga ndipo iwo akapenya. Kenako nonsenu ndi maanja anu onse mudze kwa ine.” info
التفاسير:

external-link copy
94 : 12

وَلَمَّا فَصَلَتِ ٱلۡعِيرُ قَالَ أَبُوهُمۡ إِنِّي لَأَجِدُ رِيحَ يُوسُفَۖ لَوۡلَآ أَن تُفَنِّدُونِ

Ndipo aulendo pamene adamuka (kubwerera kwawo). Bambo wawo (yemwe adali ku Kenani) adati: “Ndikumva fungo la Yûsuf pakadapanda kuti muli ndi chikhulupiliro choti ndasokonezeka nzeru, (mukadandikhulupirira)” info
التفاسير:

external-link copy
95 : 12

قَالُواْ تَٱللَّهِ إِنَّكَ لَفِي ضَلَٰلِكَ ٱلۡقَدِيمِ

(Iwo) adati: “Tikulumbira Allah! Ndithu muli mkusokera kwanu kwa kale (pokonda Yûsuf kuposa ife).” info
التفاسير: