ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمه‌ى چوایی - خالد ابراهیم بيتالا

شماره صفحه:close

external-link copy
80 : 16

وَٱللَّهُ جَعَلَ لَكُم مِّنۢ بُيُوتِكُمۡ سَكَنٗا وَجَعَلَ لَكُم مِّن جُلُودِ ٱلۡأَنۡعَٰمِ بُيُوتٗا تَسۡتَخِفُّونَهَا يَوۡمَ ظَعۡنِكُمۡ وَيَوۡمَ إِقَامَتِكُمۡ وَمِنۡ أَصۡوَافِهَا وَأَوۡبَارِهَا وَأَشۡعَارِهَآ أَثَٰثٗا وَمَتَٰعًا إِلَىٰ حِينٖ

Ndipo Allah adakuikirani nyumba zanu kuti zikhale mokhala (mwanu), ndiponso adakupangirani zikopa za ziweto (kukhala zotheka kuzikonza) kukhala nyumba, zomwe mumaziona kuti nzopepuka kuzitenga panthawi Ya ulendo wanu ndi panthawi ya kukhazikika kwanu (pamalo); ndipo kuchokera ku bweya wake wautaliutali ndi bweya wake wa manyunyu (ung’onoung’ono), ndi tsitsi lake (la ziwetozo,) mumakonza ziwiya (zovala) zosangalatsa, kwa kanthawi. info
التفاسير:

external-link copy
81 : 16

وَٱللَّهُ جَعَلَ لَكُم مِّمَّا خَلَقَ ظِلَٰلٗا وَجَعَلَ لَكُم مِّنَ ٱلۡجِبَالِ أَكۡنَٰنٗا وَجَعَلَ لَكُمۡ سَرَٰبِيلَ تَقِيكُمُ ٱلۡحَرَّ وَسَرَٰبِيلَ تَقِيكُم بَأۡسَكُمۡۚ كَذَٰلِكَ يُتِمُّ نِعۡمَتَهُۥ عَلَيۡكُمۡ لَعَلَّكُمۡ تُسۡلِمُونَ

Ndipo mwa zina zomwe Allah adapanga, adakupangirani zodzetsa mthunzi; ndipo adakupangirani mokhala kumapiri (monga mapanga akuluakulu). Adakupangiraninso nsalu (zathonje ndi ubweya) zokutetezani ku kutentha (ndi kuzizira), ndiponso (adakupangirani) zovala (za chitsulo) zokutetezani pankhondo zanu. Umo ndi momwe akukukwaniritsirani chisomo Chake kuti mugonjere (Iye). info
التفاسير:

external-link copy
82 : 16

فَإِن تَوَلَّوۡاْ فَإِنَّمَا عَلَيۡكَ ٱلۡبَلَٰغُ ٱلۡمُبِينُ

Koma ngati anyoza, basi palibe udindo wina pa iwe koma kufikitsa uthenga womveka (popanda kubisapo kalikonse). info
التفاسير:

external-link copy
83 : 16

يَعۡرِفُونَ نِعۡمَتَ ٱللَّهِ ثُمَّ يُنكِرُونَهَا وَأَكۡثَرُهُمُ ٱلۡكَٰفِرُونَ

Akuchidziwa chisomo cha Allah; koma akuchikana, ndipo ambiri a iwo ngosakhulupirira. info
التفاسير:

external-link copy
84 : 16

وَيَوۡمَ نَبۡعَثُ مِن كُلِّ أُمَّةٖ شَهِيدٗا ثُمَّ لَا يُؤۡذَنُ لِلَّذِينَ كَفَرُواْ وَلَا هُمۡ يُسۡتَعۡتَبُونَ

Ndipo (akumbutse za) tsiku lomwe tidzautsa mboni mu mtundu uliwonse; kenako sikudzaloledwa, kwa amene sadakhulupirire, (kupereka madandaulo) ndipo iwo sadzauzidwa kuti afunefune chiyanjo cha Allah (koma chilango basi). info
التفاسير:

external-link copy
85 : 16

وَإِذَا رَءَا ٱلَّذِينَ ظَلَمُواْ ٱلۡعَذَابَ فَلَا يُخَفَّفُ عَنۡهُمۡ وَلَا هُمۡ يُنظَرُونَ

Ndipo amene achita zoipa akadzachiona chilango (ndikuyamba kudandaula ndi kulira), sichidzachepetsedwa kwa iwo (chilangocho), ndipo sadzapatsidwa mwayi wina. info
التفاسير:

external-link copy
86 : 16

وَإِذَا رَءَا ٱلَّذِينَ أَشۡرَكُواْ شُرَكَآءَهُمۡ قَالُواْ رَبَّنَا هَٰٓؤُلَآءِ شُرَكَآؤُنَا ٱلَّذِينَ كُنَّا نَدۡعُواْ مِن دُونِكَۖ فَأَلۡقَوۡاْ إِلَيۡهِمُ ٱلۡقَوۡلَ إِنَّكُمۡ لَكَٰذِبُونَ

Ndipo amene ankam’phatikiza Allah akadzawaona aphatikizi awowo adzati: “Mbuye wathu! Awa ndiaphatikizi athu omwe tidali kuwapembedza m’malo mwa Inu.” Ndipo (aphatikiziwo akadzamva mawu awa) adzawaponyera mawu awo (nkunena kuti): “Ndithu inu ndi abodza.” info
التفاسير:

external-link copy
87 : 16

وَأَلۡقَوۡاْ إِلَى ٱللَّهِ يَوۡمَئِذٍ ٱلسَّلَمَۖ وَضَلَّ عَنۡهُم مَّا كَانُواْ يَفۡتَرُونَ

Ndipo tsiku limenelo onse adzadzitula kwa Allah; ndipo zidzawataika zomwe adali kuzipeka. info
التفاسير: