আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা

Al-Lail

external-link copy
1 : 92

وَٱلَّيۡلِ إِذَا يَغۡشَىٰ

Ndikulumbilira usiku pamene ukuphimba (chilichonse). info
التفاسير:

external-link copy
2 : 92

وَٱلنَّهَارِ إِذَا تَجَلَّىٰ

Ndi usana pamene kukuyera. info
التفاسير:

external-link copy
3 : 92

وَمَا خَلَقَ ٱلذَّكَرَ وَٱلۡأُنثَىٰٓ

Ndiponso Yemwe adalenga chachimuna ndi chachikazi. info
التفاسير:

external-link copy
4 : 92

إِنَّ سَعۡيَكُمۡ لَشَتَّىٰ

Ndithu zochita zanu nzosiyanasiyana.[446] info

[446] Tanthauzo lake ndikuti mwa anthu alipo ena amene amachita zabwino ndipo ena amachita zoipa. Ena amagwira ntchito zothandiza pambuyo pa imfa pamodzi ndi kutumikira Allah. Ndipo pali ena omwe amangokhala otanganidwa ndi zadziko lapansi. Ena amachita zinthu zopindula pomwe ena satero.

التفاسير:

external-link copy
5 : 92

فَأَمَّا مَنۡ أَعۡطَىٰ وَٱتَّقَىٰ

Tsono yemwe akupereka (pa njira ya Allah) ndikumamuopa (Mbuye wake ndikupewa zoletsedwa),[447] info

[447] Tanthauzo lake apa ndikupereka chuma ndi kudzipereka pa zauzimu. Ndiye kuti munthu agwiritsire ntchito chuma chake m’njira ya Allah ndiponso kwa anthu anzake. Ayeneranso kudzipereka iye mwini pa moyo wauzimu.

التفاسير:

external-link copy
6 : 92

وَصَدَّقَ بِٱلۡحُسۡنَىٰ

Ndikumavomereza zinthu zabwino; (komwe kuli kukhulupirira Allah mwanzeru),[448] info

[448] Tanthauzo la “Kuvomereza zinthu zabwino” ndiko kugwirizana nazo zimene Allah walamula, chifukwa chakuti Iye amalamula zinthu zabwino zokhazokha ndikuletsa zoipa.

التفاسير:

external-link copy
7 : 92

فَسَنُيَسِّرُهُۥ لِلۡيُسۡرَىٰ

Choncho timufewetsera njira yompititsa ku zabwino.[449] info

[449] Tanthauzo la Ayah imeneyi ndikuti: Timufewetsera njira yochitira zinthu zabwino mpaka kufikira kuti akapanda kuchita chinthu chabwino sapeza mtendere mu mtima mwake.

التفاسير:

external-link copy
8 : 92

وَأَمَّا مَنۢ بَخِلَ وَٱسۡتَغۡنَىٰ

Koma uyo achite umbombo ndikuganiza za kuti iye payekha ngokwana; info
التفاسير:

external-link copy
9 : 92

وَكَذَّبَ بِٱلۡحُسۡنَىٰ

Ndi kumatsutsa zinthu zabwino, info
التفاسير: