[110] Apa tsopano akufotokoza mmene chuma chamasiye angachigawire ponena kuti m’Chisilamu akazi akuwalola kuwagawirako chuma cha abale awo, osati kuti amuna okha ndiwo, owagawira. Koma gawo lomwe mkazi amapatsidwa limacheperapo poyerekeza ndi gawo lomwe mwamuna amalandira. Chifukwa chakuti mwamuna ndiye ali ndi udindo waukulu poyerekeza ndi mkazi. Mwamuna ali ndi udindo woyang’anira mkazi wake, ana ake ndi makolo ake. Koma mkazi alibe udindo woyang’anira mwamuna wake. Ndiponso alibe udindo woyang’anira mwana kapena makolo ake, pokhapokha ngati tate wa anawo ali wochepa nzeru. Zikatero mpomwe mkaziyo amakhala ndi udindo woyang’anira ana ake.