আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চিচেৱা অনুবাদ- খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা

Al-lsrâ’

external-link copy
1 : 17

سُبۡحَٰنَ ٱلَّذِيٓ أَسۡرَىٰ بِعَبۡدِهِۦ لَيۡلٗا مِّنَ ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِ إِلَى ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡأَقۡصَا ٱلَّذِي بَٰرَكۡنَا حَوۡلَهُۥ لِنُرِيَهُۥ مِنۡ ءَايَٰتِنَآۚ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡبَصِيرُ

۞ Ulemelero ngwa Yemwe adayendetsa kapolo Wake usiku (umodzi) kuchokera mu Msikiti Wopatulika (wa Makka) kupita ku Msikiti wakutali (wa Baitul-Muqaddas), womwe tidazidalitsa zomwe zauzungulira. (Tidampititsa kumeneko) kuti timsonyeze zina mwa zisonyezo Zathu; ndithu Iye (Allah) Ngwakumva, Ngowona ( chilichonse).[253] info

[253] Mneneri Muhammad (s.a.w) pamene adakwezedwa kumwamba adaona zisonyezo zikuluzikulu za Allah monga Munda wa mtendere, Moto, mtengo wotchedwa Sidratul- Muntaha, Angelo, Aneneri ndi zina zododometsa.

التفاسير:

external-link copy
2 : 17

وَءَاتَيۡنَا مُوسَى ٱلۡكِتَٰبَ وَجَعَلۡنَٰهُ هُدٗى لِّبَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ أَلَّا تَتَّخِذُواْ مِن دُونِي وَكِيلٗا

Ndipo Mûsa tidampatsa buku (la Taurat) tidaliika kukhala chiongoko kwa ana a Israyeli (Allah adawauza): “Musadzipangire atetezi kusiya Ine.” info
التفاسير:

external-link copy
3 : 17

ذُرِّيَّةَ مَنۡ حَمَلۡنَا مَعَ نُوحٍۚ إِنَّهُۥ كَانَ عَبۡدٗا شَكُورٗا

(Ndiponso adawauza kuti: “E inu) Mbumba ya amene tidawanyamula pamodzi ndi Nuh! (Khalani othokoza monga tate wanu.) Ndithu iye adali kapolo wothokoza kwambiri.” info
التفاسير:

external-link copy
4 : 17

وَقَضَيۡنَآ إِلَىٰ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ فِي ٱلۡكِتَٰبِ لَتُفۡسِدُنَّ فِي ٱلۡأَرۡضِ مَرَّتَيۡنِ وَلَتَعۡلُنَّ عُلُوّٗا كَبِيرٗا

Ndipo tidawazindikiritsa ana a Israyeli m’bukulo, kuti: “Ndithu inu muononga pa dziko kawiri, ndipo mudzapyola malire pochita zoipa, kupyola malire kwakukulu. info
التفاسير:

external-link copy
5 : 17

فَإِذَا جَآءَ وَعۡدُ أُولَىٰهُمَا بَعَثۡنَا عَلَيۡكُمۡ عِبَادٗا لَّنَآ أُوْلِي بَأۡسٖ شَدِيدٖ فَجَاسُواْ خِلَٰلَ ٱلدِّيَارِۚ وَكَانَ وَعۡدٗا مَّفۡعُولٗا

Ndipo likadzafika lonjezo (lakupatsidwa chilango chakuononga) koyamba mkuononga kuwiriko, tidzawakhwirizira pa inu anthu athu, eni kumenya nkhondo mwaukali, adzakhala akuzungulira mkatikati mwa nyumba (zanu), ndipo lidali lonjezo lochitika. info
التفاسير:

external-link copy
6 : 17

ثُمَّ رَدَدۡنَا لَكُمُ ٱلۡكَرَّةَ عَلَيۡهِمۡ وَأَمۡدَدۡنَٰكُم بِأَمۡوَٰلٖ وَبَنِينَ وَجَعَلۡنَٰكُمۡ أَكۡثَرَ نَفِيرًا

Kenako tidakubwezerani kupambana pa iwo (omwe adakugonjetsani poyamba); ndipo tidakupatsani chuma ndi ana, ndi kukudalitsani kukhala ndi gulu lochuluka. info
التفاسير:

external-link copy
7 : 17

إِنۡ أَحۡسَنتُمۡ أَحۡسَنتُمۡ لِأَنفُسِكُمۡۖ وَإِنۡ أَسَأۡتُمۡ فَلَهَاۚ فَإِذَا جَآءَ وَعۡدُ ٱلۡأٓخِرَةِ لِيَسُـُٔواْ وُجُوهَكُمۡ وَلِيَدۡخُلُواْ ٱلۡمَسۡجِدَ كَمَا دَخَلُوهُ أَوَّلَ مَرَّةٖ وَلِيُتَبِّرُواْ مَا عَلَوۡاْ تَتۡبِيرًا

(Tidati kwa iwo): “Ngati muchita bwino (pomumvera Allah), ubwino ngwanu (pa dziko lapansi ndi pa tsiku la Chimaliziro); ngati muipitsa (ponyoza Allah), kuipako kuli pa inu nokha. Choncho pamene idadza nthawi ya lonjezo lachilango chomaliza, (tidakutumizirani adani anu) kuti apereke kunyozeka pa nkhope zanu, ndikutinso alowe mu Nsikiti monga adalowera mnthawi yoyamba, ndikuti aononge chilichonse chimene achigonjetsa; kuononga kwakukulu.” info
التفاسير: